Numeri 9:1-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo Yehova ananena ndi Mose m'cipululu ca Sinai, mwezi woyamba wa caka caciwiri ataturuka m'dziko la Aigupto, ndi kuti,

2. Ana a Israyeli acite Paskha pa nyengo yoikidwa.

3. Tsiku lakhumi ndi cinai la mweziwo, madzulo, muziucita, pa nyengo yace yoikidwa; muucite monga mwa malemba ace onse, ndi maweruzo ace onse.

4. Ndipo Mose ananena ndi ana a Israyeli, kuti acite Paskha.

5. Ndipo anacita Paskha mwezi woyamba, tsiku lakhumi ndi cinai la mweziwo, madzulo, m'cipululu ca Sinai; monga mwa zonse Yehova adauza Mose, momwemo ana a Israyeli anacita.

Numeri 9