Numeri 32:8-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. Anatero makolo anu, muja ndinawatumiza acoke ku Kadesi Barinea kukaona dziko.

9. Popeza atakwera kumka ku cigwa ca Esikolo, naona dziko, anafoketsa mtima wa ana a Israyeli, kuti asalowe dzikoli Yehova adawapatsa.

10. Ndipo Yehova anapsa mtima tsiku lija, nalumbira iye, nati,

11. Anthu adakwerawo kuturuka m'Aigupto, kuyambira wa zaka makumi awiri ndi mphambu sadzaona dziko limene ndinalumbirira Abrahamu, ndi Isake, ndi Yakobo; popeza sananditsata Ine ndi mtima wonse;

12. koma Kalebi mwana wa Yefune, Mkenizi, ndi Yoswa mwana wa Nuni ndiwo; popeza anatsata Yehova ndi mtima wonse.

Numeri 32