Numeri 22:10-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. Ndipo Balamu anati kwa Mulungu, Balaki mwana wa Zipori mfumu ya Moabu, anatumiza kwa ine, ndi kuti,

11. Taonani, anthu awa adaturuka m'Aigupto aphimba nkhope ya dziko, idzatu unditembererere awa; kapena ndidzakhoza kulimbana nao nkhondo, ndi kuwapitikitsa.

12. Koma Mulungu anati kwa Balamu, Usapita nao; usatemberera anthuwa; pakuti adalitsika.

13. Ndipo Balamu anauka m'mawa, nati kwa akalonga a Balaki, Mukani ku dziko lanu; popeza Yehova andikaniza kuti ndisapite nanu,

14. Pamenepo akalonga a Moabu ananyamuka, nafika kwa Balaki, nati, Alikukana Balamu kudza nafe.

Numeri 22