Numeri 18:30-32 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

30. Cifukwa cace unene nao, Pamene mukwezako zokometsetsa zace, zidzayesedwanso kwa Alevi ngati zipatso za padwale, ndi zipatso za mopondera mphesa,

31. Ndipo muzidye pamalo ponse, inu ndi a pabanja panu; popeza ndizo mphotho yanu mwa nchito yanu m'cihema cokomanako.

32. Ndipo simudzasenzapo ucimo, mutakwezako zokometsetsa zace; ndipo musamaipsa zinthu zopatulika za ana a Israyeli, kuti mungafe.

Numeri 18