4. Ndipo anati wina ndi mnzace, Tiike mtsogoleri, tibwerere ku Aigupto.
5. Pamenepo Mose ndi Aroni anagwa nkhope pansi pamaso pa msonkhano wonse wa khamu la ana a Israyeli.
6. Ndipo Yoswa mwana wa Nuni, ndi Kalebi mwana wa Yefune, ndiwo a iwo aja adazonda dzikolo, anang'amba zobvala zao;
7. nanena ndi khamu lonse la ana a Israyeli, nati, Dziko tapitamo kulizonda, ndilo dziko lokometsetsa ndithu.
8. Yehova akakondwera nafe, adzatilowetsa m'dzikomo, ndi kutipatsa ilo; ndilo dziko moyenda mkaka ndi uci ngati madzi.
9. Cokhaci musamapikisana naye Yehova, musamaopa anthu a m'dzikomo; pakuti ndiwo mkate wathu; mthunzi wao wawacokera, ndipo Yehova ali nafe; musamawaopa.