Numeri 14:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Pamenepo khamu lonse linakweza mau ao, napfuula; ndipo anthuwo analira usikuwo.

2. Ndipo ana onse a Israyeli anadandaulira Mose ndi Aroni; ndi khamu lonse linanena nao, Mwenzi tikadafa m'dziko la Aigupto; kapena mwenzi tikadafa m'cipululu muno!

3. Ndipo Yehova atitengeranii kudza nafe kudziko kuno, kuti tigwe nalo lupanga? Akazi athu ndi makanda athu adzakhala cakudya cao; kodi sikuli bwino tibwerere ku Aigupto?

4. Ndipo anati wina ndi mnzace, Tiike mtsogoleri, tibwerere ku Aigupto.

Numeri 14