Nehemiya 7:31-37 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

31. Amuna a ku Mikimasi, zana limodzi mphambu makumi awiri kudza awiri.

32. Amuna a ku Betele ndi Ai, zana limodzi mphambu makumi awiri kudza atatu.

33. Amuna a ku Nebo winayo, makumi asanu kudza awiri.

34. Ana a Elamu winayo, cikwi cimodzi mphambu mazana awiri ndi makumi asanu kudza anai.

35. Ana a Harimu, mazana atatu mphambu makumi awiri.

36. Ana a Yeriko, mazana atatu mphambu makumi anai kudza asanu.

37. Ana a Lodi, Hadidi, ndi Ono, mazana asanu ndi awiri mphambu makumi awiri kudza mmodzi.

Nehemiya 7