Nehemiya 5:1-3 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Pamenepo panamveka kulira kwakukuru kwa anthu ndi akazi ao kudandaula pa abale ao Ayuda.

2. Popeza panali ena akuti, Ife, ana athu amuna ndi akazi, ndife ambiri; talandira tirigu, kuti tidye tikhale ndi moyo.

3. Panali enanso akuti, Tirikupereka cikole minda yathu, ndi minda yathu yampesa ndi nyumba zathu; kuti tilandire tirigu cifukwa ca njalayi.

Nehemiya 5