Mlaliki 7:18-26 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

18. Kuli kwabwino kugwira ici; indetu, usacotsepo dzanja lako pakuti yemwe aopa Mulungu adzaturuka monsemo.

19. Nzeru ilimbitsa wanzeru koposa akuru khumi akulamulira m'mudzi.

20. Pakuti kulibe wolungama pansi pano amene acita zabwino osacimwa.

21. Mau onsetu onenedwa usawalabadire; kuti usamve kapolo wako alikukutemberera;

22. pakuti kawiri kawiritu mtima wako udziwa kuti nawenso unatemberera ena.

23. Ndayesa zonsezi ndi nzeru; ndinati, Ndidzakhala wanzeru, koma inanditarikira.

24. Cakutari ndi cakuyadi adzacipeza ndani?

25. Ndinapotoka ndi mtima wanga womwe kudziwa ndi kusanthula ndi kufunafuna nzeru ndi malongosoledwe a zinthu, ndi kudziwa kuti udio ndiwo utsiru, ndi kuti kupusa ndi misala;

26. ndipo ndinapeza kanthu kowawa koposa imfa, ndiko mkazi amene ndiye msampha, mtima wace ukunga maukonde, manja ace ndiwo matangadza; yemwe Mulungu amuyesa wabwino adzapulumuka kwa iye; koma wocimwa adzagwidwa naye.

Mlaliki 7