Mlaliki 7:1-3 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Mbiri yabwino iposa zonunkhira zabwino; ndi tsiku lakumwalira liposa tsiku lakubadwa.

2. Kunka ku nyumba ya maliro kupambana kunka ku nyumba ya madyerero; pakuti kujako ndi matsiriziro a anthu onse; ndipo omwe ali ndi moyo adzakumbukirapo.

3. Cisoni ciposa kuseka; pakuti nkhope yakugwa ikonza mtima.

Mlaliki 7