Mlaliki 5:1-6 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Samalira phazi lako popita ku nyumba ya Mulungu; pakuti kuyandikira kumvera kupambana kupereka nsembe za zitsiru; pakuti sizizindikira kuti zirikucimwa.

2. Usalankhule mwanthuku mtima wako, usafulumire kunena kanthu pamaso pa Mulungu; pakuti Mulungu ali kumwamba, iwe uli pansi; cifukwa cace mau ako akhale owerengeka.

3. Pakuti loto lafika mwakucuruka nchito; ndipo mau a citsiru mwakucuruka maneno.

4. Utawinda ciwindo kwa Mulungu, usacedwe kucicita; pakuti sakondwera ndi zitsiru; cita comwe unaciwindaco.

5. Kusawinda kupambana kuwinda osacita,

6. Usalole m'kamwa mwako mucimwitse thupi lako; usanene pamaso pa mthenga kuti, Ndinaphophonya; Mulungu akwiyire mau ako cifukwa ninji, naononge nchito ya manja ako?

Mlaliki 5