4. pa khomo lakunja padzatsekeka; potsika mau akupera, wina nanyamuka polira mbalame, ndipo akazi onse akuyimba sadzamveka bwino;
5. inde, adzaopa za pamwamba, panjira padzakhala zoopsya; mciu nudzaphuka, dzombe ndi kukoka miyendo, zilakolako ndi kutha; pakuti munthu apita kwao kwamuyaya, akulira maliro nayendayenda panja;
6. cingwe casiliva cisanaduke, ngakhale mbale yagolidi isanasweke, ngakhale mtsuko usanaphwanyike kukasupe, ngakhale njinga yotungira madzi isanatyoke kucitsime;