9. Ukacenjeza wanzeru adzakulitsa nzeru yace;Ukaphunzitsa wolungama adzaonjezera kuphunzira,
10. Ciyambi ca nzeru ndico kuopa Yehova;Kudziwa Woyerayo ndiko luntha;
11. Pakuti mwa ine masiku ako adzacuruka,Zaka za moyo wako zidzaonjezedwa.
12. Ukakhala wanzeru, si yako yako nzeruyo?Ndipo ukanyoza udzasauka wekha.