Miyambi 9:9-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. Ukacenjeza wanzeru adzakulitsa nzeru yace;Ukaphunzitsa wolungama adzaonjezera kuphunzira,

10. Ciyambi ca nzeru ndico kuopa Yehova;Kudziwa Woyerayo ndiko luntha;

11. Pakuti mwa ine masiku ako adzacuruka,Zaka za moyo wako zidzaonjezedwa.

12. Ukakhala wanzeru, si yako yako nzeruyo?Ndipo ukanyoza udzasauka wekha.

Miyambi 9