23. Anandiimika cikhalire ciyambire,Dziko lisanalengedwe.
24. Pamene panalibe zozama ndinabadwa ine,Pamene panalibe akasupe odzala madzi.
25. Mapiri asanakhazikike,Zitunda zisanapangidwe, ndinabadwa;
26. Asanalenge dziko, ndi thengo,Ngakhale ciyambi ca pfumbi la dziko.