22. Mulungu anali nane poyamba njira yace,Asanalenge zace zakale.
23. Anandiimika cikhalire ciyambire,Dziko lisanalengedwe.
24. Pamene panalibe zozama ndinabadwa ine,Pamene panalibe akasupe odzala madzi.
25. Mapiri asanakhazikike,Zitunda zisanapangidwe, ndinabadwa;
26. Asanalenge dziko, ndi thengo,Ngakhale ciyambi ca pfumbi la dziko.
27. Pamene anakhazika mlengalenga ndinali pompo;Pamene analemba pazozama kwete kwete;
28. Polimbitsa Iye thambo la kumwamba,Pokula akasupe a zozama.
29. Poikira nyanja malire ace,Kuti madzi asapitirire pa lamulo lace;Polemba maziko a dziko,