Miyambi 8:14-18 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

14. Ndine mwini uphungu ndi kudziwitsa;Ndine luntha; ndiri ndi mphamvu.

15. Mwa ine mafumu alamulira;Akazembe naweruza molungama.

16. Mwa ine akalonga ayang'anira,Ndi akuru, ngakhale oweruza onse a m'dziko,

17. Akundikonda ndiwakonda;Akundifunafuna adzandipeza.

18. Katundu ndi ulemu ziri ndi ine,Cuma cosatha ndi cilungamo.

Miyambi 8