Miyambi 4:10-13 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. Tamvera mwananga, nulandire mau anga;Ndipo zaka za moyo wako zidzacuruka.

11. Ndakuphunzitsa m'njira ya nzeru,Ndakuyendetsa m'mayendedwe olungama.

12. Mapazi ako sadzaombana ulikuyenda;Ukathamanga, sudzapunthwa.

13. Gwira mwambo, osauleka;Uusunge; pakuti ndiwo moyo wako.

Miyambi 4