10. Tamvera mwananga, nulandire mau anga;Ndipo zaka za moyo wako zidzacuruka.
11. Ndakuphunzitsa m'njira ya nzeru,Ndakuyendetsa m'mayendedwe olungama.
12. Mapazi ako sadzaombana ulikuyenda;Ukathamanga, sudzapunthwa.
13. Gwira mwambo, osauleka;Uusunge; pakuti ndiwo moyo wako.