Miyambi 31:4-9 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Mafumu, Lemueli, mafumu sayenera kumwa vinyo;Akalonga sayenera kunena, Cakumwa caukali ciri kuti?

5. Kuti angamwe, naiwale malamulo,Naweruze mokhota anthu onse osautsidwa.

6. Wofuna kufa umpatse cakumwa caukali,Ndi vinyo kwa owawa mtima;

7. Amwe, narwale umphawi wace, Osakumbukiranso bvuto lace.

8. Tsegula pakamwa pako, ukanenere wosalankhula,Ndi mlandu wa amasiye onse.

9. Tsegula pakamwa pako,Nuweruze molungama, nunenere osauka ndi aumphawi.

Miyambi 31