Miyambi 31:27-31 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

27. Ayang'anira mayendedwe a banja lace,Sadya zakudya za ulesi.

28. Anace adzanyamuka, nadzamucha wodala;Mwamuna wace namtama, nati,

29. Ana akazi ambiri anacita mwangwiro,Koma iwe uposa onsewo.

30. Kukongola kungonyenga, maonekedwe okoma ndi cabe;Koma mkazi woopa Yehova adzatamandidwa.

31. Mumpatse zipatso za manja ace; Ndi nchito zace zimtame kubwalo.

Miyambi 31