27. Ayang'anira mayendedwe a banja lace,Sadya zakudya za ulesi.
28. Anace adzanyamuka, nadzamucha wodala;Mwamuna wace namtama, nati,
29. Ana akazi ambiri anacita mwangwiro,Koma iwe uposa onsewo.
30. Kukongola kungonyenga, maonekedwe okoma ndi cabe;Koma mkazi woopa Yehova adzatamandidwa.
31. Mumpatse zipatso za manja ace; Ndi nchito zace zimtame kubwalo.