22. Cifukwa ca kapolo pamene ali mfumu;Ndi citsiru citakhuta zakudya;
23. Cifukwa ca mkazi wodedwa wokwatidwa;Ndi mdzakazi amene adzalandira colowa ca mbuyace.
24. Ziripo zinai ziri zazing'ono padziko;Koma zipambana kukhala zanzeru:
25. Nyerere ndi mtundu wosalimba,Koma zitengeratu zakudya zao m'malimwe.
26. Mbira ndi mtundu wopanda mphamvu,Koma ziika nyumba zao m'matanthwe.