Miyambi 30:22-26 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

22. Cifukwa ca kapolo pamene ali mfumu;Ndi citsiru citakhuta zakudya;

23. Cifukwa ca mkazi wodedwa wokwatidwa;Ndi mdzakazi amene adzalandira colowa ca mbuyace.

24. Ziripo zinai ziri zazing'ono padziko;Koma zipambana kukhala zanzeru:

25. Nyerere ndi mtundu wosalimba,Koma zitengeratu zakudya zao m'malimwe.

26. Mbira ndi mtundu wopanda mphamvu,Koma ziika nyumba zao m'matanthwe.

Miyambi 30