Miyambi 3:10-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. Motero nkhokwe zako zidzangoti the,Mbiya zako zidzasefuka vinyo.

11. Mwananga, usapeputse mwambo wa Yehova,Ngakhale kutopa ndi kudzudzula kwace;

12. Pakuti Yehova adzudzula omwe awakonda;Monga atate mwana amene akondwera naye.

13. Wodala ndi wopeza nzeru,Ndi woona luntha;

14. Pakuti malonda a nzeru aposa malonda a siliva,Phindu lace liposa golidi woyengeka.

Miyambi 3