10. Motero nkhokwe zako zidzangoti the,Mbiya zako zidzasefuka vinyo.
11. Mwananga, usapeputse mwambo wa Yehova,Ngakhale kutopa ndi kudzudzula kwace;
12. Pakuti Yehova adzudzula omwe awakonda;Monga atate mwana amene akondwera naye.
13. Wodala ndi wopeza nzeru,Ndi woona luntha;
14. Pakuti malonda a nzeru aposa malonda a siliva,Phindu lace liposa golidi woyengeka.