Miyambi 29:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Yemwe aumitsa khosi atadzudzulidwa kwambiri,Adzasweka modzidzimuka, palibe comciritsa.

2. Pocuruka olungama anthu akondwa;Koma polamulira woipa anthu ausa moyo.

3. Mwamuna wokonda nzeru akondweretsa atate wace;Koma wotsagana ndi akazi adama amwaza cuma.

4. Mfumu akhazikitsa dziko ndi ciweruzo;Koma wosonkhetsa anthu mphatso alipululutsa.

Miyambi 29