Miyambi 27:3-7 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. Mwala ulemera, mcenga ndiwo katundu;Koma mkwiyo wa citsiru upambana kulemera kwace.

4. Kupweteka mtima nkwa nkhanza, mkwiyo usefuka;Koma ndani angalakike ndi nsanje?

5. Cidzudzulo comveka ciposa cikondi cobisika.

6. Kulasa kwa bwenzi kulikokhulupirika;Koma mdani apsompsona kawiri kawiri.

7. Mtima wokhuta upondereza cisa ca uci;Koma wakumva njala ayesa zowawa zonse zotsekemera.

Miyambi 27