3. Mwala ulemera, mcenga ndiwo katundu;Koma mkwiyo wa citsiru upambana kulemera kwace.
4. Kupweteka mtima nkwa nkhanza, mkwiyo usefuka;Koma ndani angalakike ndi nsanje?
5. Cidzudzulo comveka ciposa cikondi cobisika.
6. Kulasa kwa bwenzi kulikokhulupirika;Koma mdani apsompsona kawiri kawiri.
7. Mtima wokhuta upondereza cisa ca uci;Koma wakumva njala ayesa zowawa zonse zotsekemera.