Miyambi 26:13-18 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. Wolesi ati, Mkango uli panjira,Wobangulawo uli m'makwalala.

14. Monga citseko cikankhikira pa zitsulo za pamphuthu,Momwemo wolesi agubuduka pakama pace.

15. Wolesi alonga dzanja lace m'mbale;Kumtopetsa kulibweza kukamwa kwace.

16. Wolesi adziyesa wanzeruKoposa anthu asanu ndi awiri akuyankha mozindikira.

17. Wakungopita ndi kubvutika ndi ndeu yosakhala yaceAkunga wogwira makutu a garu.

18. Monga woyaruka woponya nsakali,Mibvi, ndi imfa,

Miyambi 26