Miyambi 25:1-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Iyinso ndiyo miyambo ya SolomoImene anthu a Hezekiya mfumu ya Yuda anailemba.

2. Kubisa kanthu ndi ulemerero wa Mulungu;Koma ulemerero wa mafumu ndi kusanthula kanthu.

3. Pamlengalenga patarika, ndi padziko pakuya,Koma mitima ya mafumu singasanthulike.

4. Cotsera siliva mphala yace,Mmisiri wa ng'anjo aturutsamo mbale;

5. Cotsera woipa pamaso pa mfumu,Mpando wace udzakhazikika m'cilungamo.

Miyambi 25