Miyambi 24:20-25 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

20. Pakuti woipayo sadzalandira mphotho;Nyali ya amphulupulu idzazima.

21. Mwananga, opa Yehova ndi mfumu yomwe,Osadudukira anthu osinthasintha.

22. Pakuti tsoka lao lidzaoneka modzidzimuka;Ndipo ndani adziwa cionongeko ca zaka zao?

23. Izinso ziri za anzeru.Poweruza cetera siliri labwino.

24. Wonenakwa woipa, Wolungama iwe;Magulu a anthu adzamtemberera, mitundu ya anthu idzamkwiyira,

25. Omwe amdzudzula adzasekera,Nadzadalitsika ndithu.

Miyambi 24