Miyambi 23:6-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Usadye zakudya zace za wa maso ankhwenzule,Ngakhale kukhumba zolongosoka zace;

7. Pakuti monga asinkha m'kati mwace, ali wotere;Ati kwa iwe, Idya numwe;Koma mtima wace suli pa iwe.

8. Pakuti nthongo imene unaidya udzaisanza,Ndi kutaya mau ako okondweretsa.

9. Usalankhule m'makutu a wopusa;Pakuti adzapeputsa nzeru ya mau ako.

10. Usasunthe cidziwitso cakale ca m'malire;Ngakhale kulowa m'minda ya amasiye;

Miyambi 23