Miyambi 23:23-28 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

23. Gula ntheradi, osaigulitsa;Nzeru, ndi mwambo, ndi luntha.

24. Atate wa wolungama adzasekeradi;Wobala mwana wanzeru adzakondwera naye.

25. Atate wako ndi amako akondwere,Amako wakukubala asekere.

26. Mwananga, undipatse mtima wako,Maso ako akondwere ndi njira zanga,

27. Pakuti mkazi wadama ndiye dzenje lakuya;Ndipo mkazi waciwerewere ndiye mbuna yopapatiza.

28. Pakuti abisalira ngati wacifwamba,Nacurukitsa anthu a ciwembu.

Miyambi 23