23. Gula ntheradi, osaigulitsa;Nzeru, ndi mwambo, ndi luntha.
24. Atate wa wolungama adzasekeradi;Wobala mwana wanzeru adzakondwera naye.
25. Atate wako ndi amako akondwere,Amako wakukubala asekere.
26. Mwananga, undipatse mtima wako,Maso ako akondwere ndi njira zanga,
27. Pakuti mkazi wadama ndiye dzenje lakuya;Ndipo mkazi waciwerewere ndiye mbuna yopapatiza.
28. Pakuti abisalira ngati wacifwamba,Nacurukitsa anthu a ciwembu.