10. Ukainga wonyoza, makangano adzaturuka;Makani ndi manyazi adzalekeka.
11. Wokonda kuyera mtima,Mfumu idzakhala bwenzi lace cifukwa ca cisomo ca milomo yace.
12. Maso a Yehova acinjiriza wodziwa;Koma agwetsa mau a munthu wa ziwembu.
13. Waulesi ati, Pali mkango panjapo,Ndidzaphedwa pamakwalalapo.
14. M'kamwa mwa mkazi waciwerewere muli dzenje lakuya;Yemwe Yehova amkwiyira adzagwamo.
15. Utsiru umangidwa mumtima mwa mwana;Koma ntyole yomlangira idzauingitsira kutari.