Miyambi 22:10-15 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. Ukainga wonyoza, makangano adzaturuka;Makani ndi manyazi adzalekeka.

11. Wokonda kuyera mtima,Mfumu idzakhala bwenzi lace cifukwa ca cisomo ca milomo yace.

12. Maso a Yehova acinjiriza wodziwa;Koma agwetsa mau a munthu wa ziwembu.

13. Waulesi ati, Pali mkango panjapo,Ndidzaphedwa pamakwalalapo.

14. M'kamwa mwa mkazi waciwerewere muli dzenje lakuya;Yemwe Yehova amkwiyira adzagwamo.

15. Utsiru umangidwa mumtima mwa mwana;Koma ntyole yomlangira idzauingitsira kutari.

Miyambi 22