Miyambi 21:8-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. Wosenza cimo njira yace ikhotakhota;Koma nchito ya woyera mtima ilungama.

9. Kukhala pa ngondya ya tsindwi kufunikaKuposa kukhala m'nyumba ndi mkazi wolongolola.

10. Wamphulupulu mtima wace umkhumba zoipa;Sakomera mtima mnzace.

11. Polangidwa wonyoza, wacibwana alandira nzeru,Naphunzira pakuyang'ana pa wanzeru.

12. Wolungama aganizira za nyumba ya wamphulupulu,Kuti amphulupulu amagwetsedwa, naona zoipa.

Miyambi 21