14. Mphatso ya m'tseri ipembedza mkwiyo,Ndi mtulo wa pamfunga ukali wolimba.
15. Kucita ciweruzo kukondweretsa wolungama;Koma kuwaononga akucita mphulupulu,
16. Munthu wosocera pa njira ya nzeruAdzakhala m'msonkhano wa akufa.
17. Wokonda zoseketsa adzasauka;Wokonda vinyo ndi mafuta sadzalemera.
18. Wocimwa ndiye ciombolo ca wolungama;Ndipo waciwembu adzalowa m'malo mwa oongoka mtima.
19. Kukhala m'cipululu kufunikaKuposa kukhala ndi mkazi wolongolola ndi wong'ung'udza.