Miyambi 20:6-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Anthu ambiri abukitsa yense kukoma mtima kwace;Koma ndani angapeze munthu wokhulupirika?

7. Wolungama woyenda mwangwiro,Anace adala pambuyo pace.

8. Mfumu yokhala pa mpando waweruziraIpitikitsa zoipa zonse ndi maso ace.

9. Ndani anganene, Ndasambitsa mtima wanga,Ndayera opanda cimo?

10. Miyeso yosiyana, ndi malicero osiyana,Zonse ziwirizi zinyansa Yehova.

11. Ngakhale mwana adziwika ndi nchito zace;Ngati nchito yace iri yoyera ngakhale yolungama.

Miyambi 20