16. Tenga maraya a woperekera mlendo cikole;Woperekera mkazi wacilendo cikole umgwire mwini.
17. Zakudya za cinyengo zikondweretsa munthu;Koma pambuyo pace m'kamwa mwace mudzadzala tinsangalabwi.
18. Uphungu utsimikiza zolingalira,Ponya nkhondo utapanga upo.
19. Kazitape woyendayenda awanditsa zinsinsi;Usadudukire woyasama milomo yace.