Miyambi 20:16-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

16. Tenga maraya a woperekera mlendo cikole;Woperekera mkazi wacilendo cikole umgwire mwini.

17. Zakudya za cinyengo zikondweretsa munthu;Koma pambuyo pace m'kamwa mwace mudzadzala tinsangalabwi.

18. Uphungu utsimikiza zolingalira,Ponya nkhondo utapanga upo.

19. Kazitape woyendayenda awanditsa zinsinsi;Usadudukire woyasama milomo yace.

Miyambi 20