Miyambi 16:6-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Mphulupulu iomboledwa ndi cifundo ndi ntheradi;Apatuka pa zoipa poopa Yehova.

7. Njira za munthu zikakonda Yehova,Ayanjanitsana naye ngakhale adani ace.

8. Zapang'ono, pokhala cilungamo,Ziposa phindu lalikuru lopanda ciweruzo.

9. Mtima wa munthu ulingalira njira yace;Koma Yehova ayendetsa mapazi ace.

10. Mau a mlauli ali m'milomo ya mfumu;M'kamwa mwace simudzacita cetera poweruza.

11. Mwini muyeso ndi mulingo wolungama ndiye Yehova;Ndiyenso anapanga miyala yonse yoyesera ya m'thumba.

12. Kucita mphulupulu kunyansa mafumu;Pakuti mpando wao wakhazikika ndi cilungamo.

13. Milomo yolungama ikondweretsa mafumu;Wonena zoongoka amkonda.

14. Mkwiyo wa mfumu ndi mithenga ya imfa;Wanzeru adzaukhulula.

15. M'kuunika kwa nkhope ya mfumu muli moyo;Kukoma mtima kwace kunga mtambo wa mvula ya masika.

16. Kodi kulandira nzeru sikupambana ndi golidi,Kulandira luntha ndi kusankhika koposa siliva?

Miyambi 16