Miyambi 16:19-24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

19. Kufatsa mtima ndi osaukaKuposa kugawana zofunkha ndi onyada.

20. Wolabadira mau adzapeza bwino;Ndipo wokhulupirira Yehova adala.

21. Wanzeru mtima adzachedwa wocenjera;Ndipo kukoma kwa milomo kuyenjezera kuphunzira.

22. Nzeru ndi kasupe wa moyo kwa mwini wace;Koma mwambo wa zitsiru ndi utsiru.

23. Mtima wa wanzeru ucenjeza m'kamwa mwace,Nuphunzitsanso milomo yace.

24. Mau okoma ndiwo cisa ca uci,Otsekemera m'moyo ndi olamitsa mafupa.

Miyambi 16