Miyambi 16:17-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

17. Khwalala la oongoka mtima ndilo lakuti asiye zoipa;Wosunga njira yace acinjiriza moyo wace.

18. Kunyada kutsogolera kuonongekaMtinia wodzikuza ndi kutsogolera kupunthwa.

19. Kufatsa mtima ndi osaukaKuposa kugawana zofunkha ndi onyada.

20. Wolabadira mau adzapeza bwino;Ndipo wokhulupirira Yehova adala.

Miyambi 16