17. Khwalala la oongoka mtima ndilo lakuti asiye zoipa;Wosunga njira yace acinjiriza moyo wace.
18. Kunyada kutsogolera kuonongekaMtinia wodzikuza ndi kutsogolera kupunthwa.
19. Kufatsa mtima ndi osaukaKuposa kugawana zofunkha ndi onyada.
20. Wolabadira mau adzapeza bwino;Ndipo wokhulupirira Yehova adala.