Miyambi 14:8-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. Nzeru ya wocenjera ndiyo yakuti azindikire njira yace;Koma utsiru wa opusa ndiwo cinyengo.

9. Zitsiru zinyoza kuparamula;Koma mwa oongoka mtima muli ciyanjano.

10. Mtima udziwa kuwawa kwace kwace;Mlendo sadudukira ndi cimwemwe cace.

11. Nyumba ya oipa idzapasuka;Koma hema wa oongoka mtima adzakula.

12. Iripo njira yooneka kwa mwamuna ngati yoongoka;Koma matsiriziro ace ndi njira za imfa.

Miyambi 14