8. Nzeru ya wocenjera ndiyo yakuti azindikire njira yace;Koma utsiru wa opusa ndiwo cinyengo.
9. Zitsiru zinyoza kuparamula;Koma mwa oongoka mtima muli ciyanjano.
10. Mtima udziwa kuwawa kwace kwace;Mlendo sadudukira ndi cimwemwe cace.
11. Nyumba ya oipa idzapasuka;Koma hema wa oongoka mtima adzakula.
12. Iripo njira yooneka kwa mwamuna ngati yoongoka;Koma matsiriziro ace ndi njira za imfa.