Miyambi 13:13-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. Wonyoza mau adziononga yekha;Koma woopa malangizo adzalandira mphotho.

14. Malamulo a wanzeru ndiwo kasupe wa moyo,Apatutsa ku misampha ya imfa.

15. Nzeru yabwino ipatsa cisomo;Koma njira ya aciwembu iri makolokoto.

16. Yense wocenjera amacita mwanzeru:Koma wopusa aonetsa utsiru.

Miyambi 13