13. Wonyoza mau adziononga yekha;Koma woopa malangizo adzalandira mphotho.
14. Malamulo a wanzeru ndiwo kasupe wa moyo,Apatutsa ku misampha ya imfa.
15. Nzeru yabwino ipatsa cisomo;Koma njira ya aciwembu iri makolokoto.
16. Yense wocenjera amacita mwanzeru:Koma wopusa aonetsa utsiru.