Miyambi 12:7-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Oipa amagwa kuli zi;Koma banja la olungama limaimabe.

8. Munthu amatamandidwa monga mwa nzeru yace;Koma wokhota mtima adzanyozedwa.

9. Wonyozedwa, amene ali ndi kapolo,Aposa wodzikuza, amene asowa zakudya.

10. Wolungama asamalira moyo wa coweta cace;Koma cifundo ca oipa ndi nkhanza.

11. Zakudyazikwanira wolima minda yace;Koma wotsata anthu opanda pace asowa nzeru.

12. Woipa akhumba cokodwa ndi amphulupulu;Koma muzu wa olungama umabala zipatso.

13. M'kulakwa kwa milomo muli msampha woipa;Koma wolungama amaturuka m'mabvuto.

14. Munthu amakhuta zabwino ndi zipatso za m'kamwa mwace;Zocita za manja ace zidzabwezedwa kwa iye.

15. Njira ya citsiru nlolungama pamaso pace pace;Koma wanzeru amamvera uphungu.

16. Mkwiyo wa citsiru udziwika posacedwa;Koma wanzeru amabisa manyazi.

17. Wolankhula ntheradi aonetsa cilungamo;Koma mboni yonama imanyenga.

18. Alipo wonena mwansontho ngati kupyoza kwa lupanga;Koma lilime la anzeru lilamitsa.

19. Mlomo wa ntheradi ukhazikika nthawi zonse;Koma lilime lonama likhala kamphindi.

20. Cinyengo ciri m'mitima ya oganizira zoipa;Koma aphungu a mtendere amakondwa.

21. Palibe bvuto lidzagwera wolungama;Koma amphulupulu adzadzazidwa ndi zoipa,

Miyambi 12