7. Oipa amagwa kuli zi;Koma banja la olungama limaimabe.
8. Munthu amatamandidwa monga mwa nzeru yace;Koma wokhota mtima adzanyozedwa.
9. Wonyozedwa, amene ali ndi kapolo,Aposa wodzikuza, amene asowa zakudya.
10. Wolungama asamalira moyo wa coweta cace;Koma cifundo ca oipa ndi nkhanza.
11. Zakudyazikwanira wolima minda yace;Koma wotsata anthu opanda pace asowa nzeru.
12. Woipa akhumba cokodwa ndi amphulupulu;Koma muzu wa olungama umabala zipatso.