Miyambi 12:7-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Oipa amagwa kuli zi;Koma banja la olungama limaimabe.

8. Munthu amatamandidwa monga mwa nzeru yace;Koma wokhota mtima adzanyozedwa.

9. Wonyozedwa, amene ali ndi kapolo,Aposa wodzikuza, amene asowa zakudya.

10. Wolungama asamalira moyo wa coweta cace;Koma cifundo ca oipa ndi nkhanza.

11. Zakudyazikwanira wolima minda yace;Koma wotsata anthu opanda pace asowa nzeru.

12. Woipa akhumba cokodwa ndi amphulupulu;Koma muzu wa olungama umabala zipatso.

Miyambi 12