Miyambi 12:12-18 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

12. Woipa akhumba cokodwa ndi amphulupulu;Koma muzu wa olungama umabala zipatso.

13. M'kulakwa kwa milomo muli msampha woipa;Koma wolungama amaturuka m'mabvuto.

14. Munthu amakhuta zabwino ndi zipatso za m'kamwa mwace;Zocita za manja ace zidzabwezedwa kwa iye.

15. Njira ya citsiru nlolungama pamaso pace pace;Koma wanzeru amamvera uphungu.

16. Mkwiyo wa citsiru udziwika posacedwa;Koma wanzeru amabisa manyazi.

17. Wolankhula ntheradi aonetsa cilungamo;Koma mboni yonama imanyenga.

18. Alipo wonena mwansontho ngati kupyoza kwa lupanga;Koma lilime la anzeru lilamitsa.

Miyambi 12