Miyambi 12:11-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. Zakudyazikwanira wolima minda yace;Koma wotsata anthu opanda pace asowa nzeru.

12. Woipa akhumba cokodwa ndi amphulupulu;Koma muzu wa olungama umabala zipatso.

13. M'kulakwa kwa milomo muli msampha woipa;Koma wolungama amaturuka m'mabvuto.

14. Munthu amakhuta zabwino ndi zipatso za m'kamwa mwace;Zocita za manja ace zidzabwezedwa kwa iye.

Miyambi 12