11. Zakudyazikwanira wolima minda yace;Koma wotsata anthu opanda pace asowa nzeru.
12. Woipa akhumba cokodwa ndi amphulupulu;Koma muzu wa olungama umabala zipatso.
13. M'kulakwa kwa milomo muli msampha woipa;Koma wolungama amaturuka m'mabvuto.
14. Munthu amakhuta zabwino ndi zipatso za m'kamwa mwace;Zocita za manja ace zidzabwezedwa kwa iye.