Miyambi 10:14-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

14. Anzeru akundika zomwe adziwaKoma m'kamwa mwa citsiru muononga tsopano lino.

15. Cuma ca wolemera ndi mudzi wace wolimba;Koma umphawi wao uononga osauka.

16. Nchito za wolungama zipatsa moyo;Koma phindu la oipa licimwitsa.

17. Wosunga mwambo ali m'njira ya moyo;Koma wosiya cidzudzulo asocera.

18. Wobisa udani ali ndi milomo yonama;Wonena ugogodi ndiye citsiru.

19. Pocuruka mau zolakwa sizisoweka;Koma wokhala cete acita mwanzeru.

Miyambi 10