Mateyu 8:21-24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

21. Ndipo wina wa ophunzira ace anati kwa Iye, Ambuye, mundilole ine nditange ndamuka kuika maliro a atate wanga.

22. Koma Yesu ananena kwa iye, Tsata Ine, nuleke akufa aike akufa ao.

23. Ndipo pamene Iye atalowa m'ngalawa, ophunzira ace anamtsata Iye.

24. Ndipo onani, m panauka namondwe wamkuru panyanja, kotero kuti ngalawa inapfundidwa ndi mafunde: koma Iye anali m'tulo.

Mateyu 8