21. Ndipo wina wa ophunzira ace anati kwa Iye, Ambuye, mundilole ine nditange ndamuka kuika maliro a atate wanga.
22. Koma Yesu ananena kwa iye, Tsata Ine, nuleke akufa aike akufa ao.
23. Ndipo pamene Iye atalowa m'ngalawa, ophunzira ace anamtsata Iye.
24. Ndipo onani, m panauka namondwe wamkuru panyanja, kotero kuti ngalawa inapfundidwa ndi mafunde: koma Iye anali m'tulo.