8. pakuti yense wakupempha alandira; ndi wakufunayo apeza; ndi kwa wogogodayo citsegulldwa.
9. Kapena munthu ndani wa inu, amene pompempha mwana wace mkate, adzampatsa mwala?
10. Kapena pompempha nsomba, adzampatsa iye njoka kodi?
11. Comweco, ngati inu, muli oipa, mudziwa kupatsa ana anu mphatso zabwino, kopambana kotani nanga Atate wanu wa Kumwamba adzapatsa zinthu zabwino kwa iwo akumpempha Iye?
12. Cifukwa cace zinthu ziri zonse mukafuna kuti anthu acitire inu, inunso muwacitire iwo zotero; pakuti ico ndico cilamulo ndi aneneri.