11. Pomwepo mdierekezi anamsiya Iye, ndipo onani, angelo anadza, namtumikira Iye.
12. Ndipo pamene Yesu anamva kuti anampereka Yohane, anamuka kulowa ku Galileya;
13. ndipo anacoka ku Nazarete nadza nakhalitsa Iye m'Kapernao ira pambali pa nyanja, m'malire a Zebuloni ndi Nafitali:
14. kuti cikacitidwe conenedwa ndi Yesaya mneneri, kuti,