Mateyu 4:11-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. Pomwepo mdierekezi anamsiya Iye, ndipo onani, angelo anadza, namtumikira Iye.

12. Ndipo pamene Yesu anamva kuti anampereka Yohane, anamuka kulowa ku Galileya;

13. ndipo anacoka ku Nazarete nadza nakhalitsa Iye m'Kapernao ira pambali pa nyanja, m'malire a Zebuloni ndi Nafitali:

14. kuti cikacitidwe conenedwa ndi Yesaya mneneri, kuti,

Mateyu 4