4. nanena, Ndinacita koipa ine, pakupereka mwazi wosalakwa. Koma iwo anati, Tiri naco ciani ife? udzionere wekha.
5. Ndipo iye anataya pansi ndalamazo paKacisi, nacokapo, nadzipacika yekha pakhosi.
6. Ndipo ansembe akuru anatenga ndalamazo, nati, Sikuloledwa kuziika m'cosonkhera ndalama za Mulungu, cifukwa ndizo mtengo wa mwazi.
7. Koma anapangana, nazigula munda wa woumba mbiya, ukhale manda a alendo.
8. Cifukwa cace munda umenewu anaucha, Munda-wa-mwazi, kufikira lero lino.