Mateyu 26:16-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

16. Ndipo kuyambira pamenepo iye anafunafuna nthawi yabwino yakuti ampereke Iye.

17. Ndipo tsiku loyamba la mkate wopanda cotupitsa, ophunzira anadza kwa Yesu, nati, Mufuna tikakonzere kuti Paskha, kuti mukadye?

18. Nati Iye, Mukani kumzinda kwa munthu wangana, mukati kwa iye, Mphunzitsi anena. Nthawi yanga yayandikirai ndidzadya Paskha kwanu pamodzi ndi ophunzira anga.

19. Ndipo ophunzira anacita monga Yesu anawauza, nakonza Paskha.

20. Ndipo pakufika madzulo, Iye analikukhala pacakudya pamodzi ndi ophunzira khumi ndi awiri;

Mateyu 26