Mateyu 24:48-51 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

48. Koma kapolo woipa akanena mumtima mwace, Mbuye wanga wacedwa;

49. nadzayamba kupanda akapolo anzace, nadya ndi kumwa pamodzi ndi oledzera;

50. mbuye wa kapoloyo adzafika tsiku losamuyembekeza iye, ndi nthawi yosadziwa iye,

51. nadzamdula, nadzaika pokhala pace ndi anthu onyenga; 8 pomwepo padzakhala kulira ndi kukukuta mano.

Mateyu 24