15. Cifukwa cace m'mene mukadzaona conyansa ca kupululutsa, cimene cidanenedwa ndi Danieli mneneri, citaima m'malo oyera (iye amene awerenga m'kalata azindikire)
16. pomwepo iwo ali m'Yudeya athawire kumapiri:
17. iye ali pamwamba pa chindwi, asatsikire kunyamula za m'nyumba mwace;
18. ndi iye wa m'munda asabwere kutenga copfunda cace.
19. Koma tsoka ali nalo iwo akukhala ndi pakati, ndi akuyamwitsa ana m'masiku awo!