Mateyu 24:15-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

15. Cifukwa cace m'mene mukadzaona conyansa ca kupululutsa, cimene cidanenedwa ndi Danieli mneneri, citaima m'malo oyera (iye amene awerenga m'kalata azindikire)

16. pomwepo iwo ali m'Yudeya athawire kumapiri:

17. iye ali pamwamba pa chindwi, asatsikire kunyamula za m'nyumba mwace;

18. ndi iye wa m'munda asabwere kutenga copfunda cace.

19. Koma tsoka ali nalo iwo akukhala ndi pakati, ndi akuyamwitsa ana m'masiku awo!

Mateyu 24